DANIELE 11:31 |
Ary hisy miaramila hitsangana noho ny teniny ka handoto ny fitoerana masina, dia ny fiarovana mafy, ary hampitsahatra ny fanatitra isan'andro sady hampiditra ny fahavetavetana mahatonga fandravana.[Heb. sandry] |
|
DANIELE 12:11 |
“Kuyambira pamene nsembe ya tsiku ndi tsiku idzathetsedwa ndi kukhazikitsa kwa chonyansa chobweretsa chisokonezo chija, padzapita masiku 1,290. |
|
DEUTERONOMO 22:5 |
Akazi asavale zovala za amuna, kapena mwamuna kuvala zovala za akazi, pakuti Yehova Mulungu wanu amanyansidwa ndi aliyense wochita izi. |
|
DEUTERONOMO 23:18 |
Musabweretse malipiro a wachiwerewere wamkazi kapena wamwamuna Mʼnyumba ya Yehova Mulungu wanu kudzapereka za malumbiro aliwonse, chifukwa Yehova Mulungu wanu amadana ndi zimenezi. |
|
DEUTERONOMO 24:4 |
mwamuna wake woyamba uja, amene anamuleka saloledwanso kumukwatira kachiwiri popeza mkaziyo wadetsedwa. Chimenechi ndi chonyansa pamaso pa Yehova. Musalowetse tchimo mʼdziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani ngati cholowa chanu. |
|
YESAYA 1:13 |
Siyani kubweretsa nsembe zachabechabezo! Nsembe zanu zofukiza zimandinyansa Ine. Sindingapirire misonkhano yanu yoyipa, kapenanso zikondwerero za Mwezi Watsopano ndi Masabata. |
|
LEVITIKO 7:18 |
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo. |
|
LEVITIKO 18:22 |
“ ‘Usagonane ndi mwamuna ngati mkazi; chimenecho ndi chinthu chonyansa. |
|
MIYAMBO 11:1 |
Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa, koma amakondwera ndi muyeso woyenera. |
|
MIYAMBO 11:20 |
Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro. |
|
MIYAMBO 12:22 |
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona. |
|
MIYAMBO 15:8 |
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima. |
|
MIYAMBO 15:26 |
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa. |
|
MIYAMBO 16:5 |
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa. |
|
MIYAMBO 17:15 |
Kumasula munthu wolakwa kapena kumanga munthu wosalakwa, zonse ziwirizi Yehova zimamunyansa. |
|
MIYAMBO 20:10 |
Masikelo ndi miyeso ya zinthu imene ili yachinyengo zonsezi Yehova zimamunyansa. |
|
MIYAMBO 20:23 |
Miyeso yosintha imamunyansa Yehova; ndipo masikelo onyenga si abwino. |
|
MIYAMBO 28:9 |
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova. |
|
CHIVUMBULUTSO 21:27 |
Kanthu kosayeretsedwa sikadzalowamo, kuphatikizanso aliyense wochita zinthu zochititsa manyazi ndi zachinyengo, koma okhawo amene mayina awo alembedwa mʼbuku lamoyo la Mwana Wankhosa. |
|
MARKO 13:14 |
“Mukadzaona ‘chinthu chonyansa chosakaza’ chitayima pa malo amene si ake, owerenga azindikire. Pamenepo amene ali ku Yudeya athawire kumapiri. |
|
MATEYU 24:15 |
“Tsono mukadzaona chinthu chonyansa chosakaza chitayima pamalo oyera chimene anayankhula mneneri Danieli, owerengayo azindikire. |
|
AROMA 1:26-27 |
[26] Chifukwa cha ichi, Mulungu anawasiya kuti azitsata zilakolako zochititsa manyazi. Ngakhale akazi omwe anasiya machitidwe achibadwidwe pa za ukwati, namachita machitidwe ena otsutsana ndi chibadwa chawo.[27] Chimodzimodzinso amuna analeka machitidwe a ukwati ndi akazi nʼkumakhumbana amuna okhaokha. Amuna ankachita zochitisa manyazizi ndi amuna anzawo, ndipo analandira chilango choyenera molingana ndi zochita zawo zachitayikozo. |
|
LEVITIKO 20:12-13 |
[12] “ ‘Ngati munthu agonana ndi mkazi wa mwana wake, awiriwo ayenera kuphedwa. Iwo achita chinthu chonyansa kwambiri. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo.[13] “ ‘Ngati munthu agonana ndi mwamuna mnzake ngati akugonana ndi mkazi, ndiye kuti onsewo achita chinthu cha manyazi. Choncho aphedwe. Magazi awo adzakhala pa mitu pawo. |
|
MIYAMBO 6:16-20 |
[16] Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo, zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:[17] maso onyada, pakamwa pabodza, manja akupha munthu wosalakwa,[18] mtima wokonzekera kuchita zoyipa, mapazi othamangira msanga ku zoyipa,[19] mboni yonama yoyankhula mabodza komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.[20] Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako; ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako. |
|
Chewa Bible 2016 |
Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® |