AEFESO 4:26-31 |
[26] Kwiyani, koma musachimwe; dzuwa lisalowe muli chikwiyire,[27] ndiponso musampatse malo mdierekezi.[28] Wakubayo asabenso; koma makamaka agwiritse ntchito, nagwire ntchito yokoma ndi manja ake, kuti akhale nacho chakuchereza wosowa.[29] Nkhani yonse yovunda isatuluke m'kamwa mwanu, koma ngati pali ina yabwino kukumangirira monga mofunika ndiyo, kuti ipatse chisomo kwa iwo akumva.[30] Ndipo musamvetse chisoni Mzimu Woyera wa Mulungu, amene munasindikizidwa chizindikiro mwa Iye, kufikira tsiku la maomboledwe.[31] Chiwawo chonse, ndi kupsa mtima, ndi mkwiyo, ndi chiwawa, ndi mwano zichotsedwe kwa inu, ndiponso choipa chonse. |
|
YAKOBO 1:19-20 |
[19] Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.[20] Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu. |
|
MIYAMBO 29:11 |
Chitsiru chivumbulutsa mkwiyo wake wonse; koma wanzeru auletsa nautontholetsa. |
|
MLALIKI 7:9 |
Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'chifuwa cha zitsiru. |
|
MIYAMBO 15:1 |
Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo; koma mau owawitsa aputa msunamo. |
|
MIYAMBO 15:18 |
Munthu wozaza aputa makani; koma wosakwiya msanga atonthoza makangano. |
|
AKOLOSE 3:8 |
Koma tsopano tayani inunso zonsezi: mkwiyo, kupsa mtima, dumbo, mwano, zonyansa zotuluka m'kamwa mwanu: |
|
YAKOBO 4:1-2 |
[1] Zichokera kuti nkhondo, zichokera kuti zolimbana mwa inu? Kodi sizichokera kuzikhumbitso zanu zochita nkhondo m'ziwalo zanu?[2] Mulakalaka, ndipo zikusowani; mukupha, nimuchita kaduka, ndipo simukhoza kupeza; mulimbana, nimuchita nkhondo; mulibe kanthu, chifukwa simupempha. |
|
MIYAMBO 16:32 |
Wosakwiya msanga aposa wamphamvu; wolamulira mtima wake naposa wolanda mudzi. |
|
MIYAMBO 22:24 |
Usayanjane ndi munthu wokwiya msanga; ngakhale kupita ndi mwamuna waukali; |
|
MATEYU 5:22 |
koma Ine ndinena kwa inu, kuti yense wokwiyira mbale wake wopanda chifukwa adzakhala wopalamula mlandu; ndipo amene adzanena ndi mbale wake, Wopanda pake iwe, adzakhala wopalamula mlandu wa akulu: koma amene adzati, Chitsiru iwe: adzakhala wopalamula Gehena wamoto. |
|
MASALIMO 37:8-9 |
[8] Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo; usavutike mtima ungachite choipa.[9] Pakuti ochita zoipa adzadulidwa; koma iwo akuyembekeza Yehova, iwowa adzalandira dziko lapansi. |
|
MASALIMO 7:11 |
Mulungu ndiye Woweruza wolungama, ndiye Mulungu wakukwiya masiku onse. |
|
2 MAFUMU 11:9-10 |
[9] Ndipo atsogoleri a mazana anachita monga mwa zonse anawalamulira Yehoyada wansembe, natenga yense anthu ake olowera pa Sabata, ndi otulukira pa Sabata, nafika kwa Yehoyada wansembeyo.[10] Ndipo wansembeyo anapereka kwa atsogoleri a mazana mikondo ndi zikopa, zinali za mfumu Davide, zosungika m'nyumba ya Yehova. |
|
2 MAFUMU 17:18 |
Chifukwa chake Yehova anakwiya naye Israele kwakukulu, nawachotsa pamaso pake osatsala mmodzi, koma fuko la Yuda lokha. |
|
MIYAMBO 14:29 |
Wosakwiya msanga apambana kumvetsa; koma wansontho akuza utsiru. |
|
Chewa Bible 2014 |
Bible Society of Malawi |