1 TIMOTEO 5:8 |
Koma ngati wina sadzisungiratu mbumba yake ya iye yekha, makamaka iwo a m'banja lake, wakana chikhulupiriro iye, ndipo aipa koposa wosakhulupirira. |
|
2 AKORINTO 9:8 |
Ndipo Mulungu akhoza kuchulukitsira chisomo chonse kwa inu; kuti inu, pokhala nacho chikwaniro chonse m'zinthu zonse, nthawi zonse, mukachulukire kuntchito yonse yabwino; |
|
DEUTERONOMO 29:12 |
kuti mulowe chipangano cha Yehova Mulungu wanu, ndi lumbiriro lake, limene Yehova Mulungu wanu achita ndi inu lero lino; |
|
AEFESO 3:20 |
Ndipo kwa Iye amene angathe kuchita koposaposatu zonse zimene tizipempha, kapena tiziganiza, monga mwa mphamvu ya kuchita mwa ife, |
|
EKSODO 34:6 |
Ndipo Yehova anapita pamaso pake, nafuula, Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wachisomo, wolekereza, ndi wa ukoma mtima wochuluka, ndi wachoonadi; |
|
YAKOBO 1:17 |
Mphatso iliyonse yabwino, ndi chininkho chilichonse changwiro zichokera Kumwamba, zotsika kwa Atate wa mauniko, amene alibe chisanduliko, kapena mthunzi wa chitembenukiro. |
|
YOHANE 10:10 |
Siikudza mbala, koma kuti ikabe, ndi kupha, ndi kuononga. Ndadza Ine kuti akhale ndi moyo, ndi kukhala nao wochuluka. |
|
LUKA 6:38 |
Patsani, ndipo kudzapatsidwa kwa inu; muyeso wabwino, wotsendereka, wokuchumuka, wosefukira, anthu adzakupatsani m'manja mwanu. Pakuti kudzayesedwa kwa inu ndi muyeso womwewo muyesa nao inu. |
|
LUKA 6:45 |
Munthu wabwino atulutsa zabwino m'chuma chokoma cha mtima wake; ndi munthu woipa atulutsa zoipa m'choipa chake: pakuti m'kamwa mwake mungolankhula mwa kuchuluka kwa mtima wake. |
|
MATEYU 6:33 |
Koma muthange mwafuna Ufumu wake ndi chilungamo chake, ndipo zonse zimenezo zidzaonjezedwa kwa inu. |
|
AFILIPI 4:19 |
Koma Mulungu wanga adzakwaniritsa chosowa chanu chilichonse monga mwa chuma chake m'ulemerero mwa Khristu Yesu. |
|
MIYAMBO 3:5-10 |
[5] Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse, osachirikizika pa luntha lako;[6] umlemekeze m'njira zako zonse, ndipo Iye adzaongola mayendedwe ako.[7] Usadziyese wekha wanzeru; opa Yehova, nupatuke pazoipa;[8] mitsempha yako idzalandirapo moyo, ndi mafupa ako uwisi.[9] Lemekeza Yehova ndi chuma chako, ndi zinthu zako zonse zoyambirira kucha;[10] motero nkhokwe zako zidzangoti thee, mbiya zako zidzasefuka vinyo. |
|
MASALIMO 23:5 |
Mundiyalikira gome pamaso panga m'kuona kwa adani anga; mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka. |
|
MASALIMO 36:8 |
Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m'nyumba mwanu, ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu. |
|
MASALIMO 37:11 |
Koma ofatsa adzalandira dziko lapansi; nadzakondwera nao mtendere wochuluka. |
|
MASALIMO 65:11 |
Muveka chakachi ndi ukoma wanu; ndipo mabande anu akukha zakucha. |
|
MASALIMO 72:16 |
M'dzikomo mudzakhala dzinthu dzochuluka pamwamba pa mapiri; zipatso zake zidzati waa, ngati za ku Lebanoni, ndipo iwo a m'mudzi adzaphuka ngati msipu wapansi. |
|
AROMA 15:13 |
Ndipo Mulungu wa chiyembekezo adzaze inu ndi chimwemwe chonse ndi mtendere m'kukhulupirira, kuti mukachuluke ndi chiyembekezo, mu mphamvu ya Mzimu Woyera. |
|
MASALIMO 66:8-12 |
[8] Lemekezani Mulungu wathu, mitundu ya anthu inu, ndipo mumveketse liu la chilemekezo chake.[9] Iye amene asunga moyo wathu tingafe, osalola phazi lathu literereke.[10] Pakuti munatiyesera, Mulungu, munatiyenga monga ayenga siliva.[11] Munapita nafe kuukonde; munatisenza chothodwetsa pamsana pathu.[12] Munapititsa anthu oberekeka pamwamba pamitu pathu; tinapyola moto ndi madzi; koma munatifikitsa potitsitsimutsa. |
|
Chewa Bible 2014 |
Bible Society of Malawi |