1 PETRO 3:3-4 |
[3] Amene kukometsera kwanu kusakhale kwa kunja, kuluka tsitsi ndi kubvala za golidi, kapena kubvala cobvala;[4] koma kukhale munthu wobisika wamtima, m'cobvala cosaola ca mzimu wofatsa ndi wacete, ndiwo wa mtengo wace wapatali pamaso pa Mulungu. |
|
2 AKORINTO 4:16 |
Cifukwa cace sitifoka; koma ungakhale umunthu wathu wakunja ubvunda, wa m'kati mwathu ukonzedwa kwatsopano tsiku ndi tsiku. |
|
AEFESO 2:10 |
Pakuti ife ndife cipango cace, olengedwa mwa Kristu Yesu, kucita nchito zabwino, zimene Mulungu anazipangiratu, kuti tikayende m'menemo. |
|
GENESIS 1:27 |
Mulungu ndipo adalenga munthu m'cifanizo cace, m'cifanizo ca Mulungu adamlenga iye; adalenga iwo mwamuna ndi mkazi. |
|
YESAYA 40:8 |
Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zacikhalire. |
|
AFILIPI 4:8 |
Cotsalira, abale, zinthu ziri zonse zoona, ziri zonse zolemekezeka, ziri zonse zolungama, ziri zonse zoyera, ziri zonse zokongola, ziri zonse zimveka zokoma; ngati kuli cokoma mtima cina, kapena citamando cina, zilingirireni izi. |
|
MASALIMO 139:14 |
Ndikuyamikani cifukwa kuti cipangidwe canga ncoopsa ndi codabwiza; Nchito zanu nzodabwiza; Moyo wanga ucidziwa ici bwino ndithu. |
|
AROMA 8:6 |
pakuti cisamaliro ca thupi ciri imfa; koma cisamaliro ca mzimu ciri moyo ndi mtendere. |
|
NYIMBO YA SOLOMONI 4:7 |
Wakongola monse monse, wokondedwa wanga, namwaliwe, Mulibe cirema mwa iwe. |
|
MATEYU 6:28-29 |
[28] Ndipo muderanji nkhawa ndi cobvala? Tapenyetsani maluwa a kuthengo, makulidwe ao; sagwiritsa nchito, kapena sapota:[29] koma ndinena kwa inu, kuti angakhale Solomo mu ulemerero wace wonse sanabvala monga limodzi la amenewa. |
|
1 TIMOTEO 2:9-10 |
[9] Momwemonso, akazi adzibveke okha ndi cobvala coyenera, ndi manyazi, ndi cidziletso; osati ndi tsitsi lace loluka, ndi golidi kapena ngale, kapena maraya a mtengo wace wapatali;[10] komatu (umo mokomera akazi akubvomereza kulemekeza Mulungu), mwa nchito zabwino. |
|
1 SAMUELE 16:7 |
Koma Yehova ananena ndi Samueli, Vsayang'ane nkhope yace, kapena kutalika kwa msinkhu wace, popeza Ine ndinamkana iye; pakuti Yehova saona monga aona munthu; pakuti munthu ayang'ana cooneka ndi maso, koma Yehova ayang'ana mumtima. |
|
MLALIKI 3:11 |
Cinthu ciri conse anacikongoletsa pa mphindi yace; ndipo waika zamuyaya m'mitima yao ndipo palibe munthu angalondetse nchito Mulungu wazipanga ciyambire mpaka citsiriziro. |
|
AGALATIYA 3:26-27 |
[26] 3 Pakuti inu nonse muli ana a Mulungu, mwa cikhulupiriro ca mwa Yesu Kristu.[27] 4 Pakuti nonse amene munabatizidwa kwa Kristu mudabvala Kristu. |
|
MIYAMBO 3:15-18 |
[15] Mtengo wace uposa ngale; Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.[16] Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace; Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.[17] Njira zace ziri zokondweretsa, Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.[18] Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira; Wakulumirira ngwodala. |
|
EZEKIELE 28:17-18 |
[17] Unadzikuza mtima cifukwa ca kukongola kwako, waipsa nzeru zako; cifukwa ca kuwala kwako ndakugwetsa pansi, ndakuika pamaso pa mafumu, kuti akupenye.[18] Mwa mphulupulu zako zocuruka ndi malonda ako osalungama waipsa malo ako opatulika; cifukwa cace ndaturutsa moto m'kati mwako wakunyeketsa iwe; ndipo ndakusandutsa mapulusa panthaka pamaso pa onse akuona. |
|
YAKOBO 1:23 |
Pakuti ngati munthu ali wakumva mau wosati wakucita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang'anira nkhope yace ya cibadwidwe cace m'kalirole; |
|
MATEYU 23:28 |
Comweco inunso muonekera olungama pamaso pa anthu, koma m'kati muli odzala ndi cinyengo ndi kusayeruzika. |
|
MIYAMBO 31:30 |
Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi cabe; Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa. |
|
Chewa Bible (BL) 1992 |
Zambia Bible Society, Malawi Bible Society and Zimbabwe Bible Society |