1 TIMOTEO 5:4 |
Koma ngati wamasiye wina ali nao ana kapena adzukulu, ayambe aphunzire iwo kucitira ulemu a m'banja lao, ndi kubwezera akuwabala; pakuti ici ncolandirika pamaso pa Mulungu. |
|
1 TIMOTEO 3:15 |
kuti udziwe kuyenedwa kwace pokhala m'nyumba ya Mulungu, ndiye Eklesia wa Mulungu wamoyo, mzati ndi mcirikizo wa coonadi. |
|
YOHANE 8:32 |
ndipo mudzazindikira coonadi, ndipo coonadi cidzakumasulani. |
|
CHIVUMBULUTSO 17:5 |
ndipo pamphumi pace padalembedwa dzina, CINSINSI, BABULO WAUKURU AMAI WA ACIGOLOLO NDI WA ZONY ANSITSA ZA DZIKO. |
|
YAKOBO 1:27 |
Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: z kuceza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m'cisautso cao, ndi 1 kudzisungira mwini wosacitidwa mawanga ndi dziko lapansi. |
|
YOHANE 6:54 |
11 Iye wakudya thupi langa ndi kumwa mwazi wanga ali nao moyo wosatha; ndipo Ine ndidzamuukitsa iye tsiku lomariza. |
|
MARKO 6:3 |
Si mmisiri wa mitengo uyu, mwana wa Mariya, mbale wao wa Yakobo, ndi Yose, ndi Yuda, ndi Simoni? Ndipo alongo ace sali nafe pano kodi? Ndipo anakhumudwa ndi Iye. |
|
YOHANE 14:6 |
Yesu ananena naye, ine ndinenjira, ndi coonadi, ndi moyo. Palibe munthu adza kwa Atate, koma mwa Ine. |
|
GENESIS 1:1-7 |
[1] PACIYAMBI Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi.[2] Dziko lapansi ndipo linali lopanda kanthu; ndipo mdima unali pamwamba pa nyanja; ndipo mzimu wa Mulungu unaliokufungatira pamwamba pa madzi.[3] Ndipo anati Mulungu, Kuyere; ndipo kunayera.[4] Ndipo anaona Mulungu kuti kuyerako kunali kwabino: ndipo Mulungu analekanitsa kuyera ndi mdima.[5] Ndipo Mulungu anacha kuyerako Usana, ndi mdimawo anaucha Usiku. Ndipo panali madzulo ndipo panali m'mawa, tsiku loyamba.[6] Ndipo anati Mulungu, Pakhale thambo pakati pa madzi, lilekanitse madzi ndi madzi.[7] Ndipo Mulungu anapanga thambo, nalekanitsa madzi anali pansi pa thambolo ndi madzi analf pamwamba pa thambolo: ndipo kunatero. |
|
1 TIMOTEO 5:8 |
Koma ngati wina sadzisungiratu mbumba yace ya iye yekha, makamaka iwo a m'banja lace, wakana cikhulupiriro iye, ndipo aipa koposa wosakhulupira. |
|
AGALATIYA 1:19 |
Koma wina wa atumwi sindinamuona, koma Yakobo mbale wa Ambuye. |
|
MALAKI 1:11 |
Pakuti kuyambira koturukira dzuwa kufikira kolowera kwace dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu; ndipo m'malo monse adzaperekera dzina langa cofukiza ndi copereka coona; pakuti dzina langa lidzakhala lalikuru mwa amitundu, ati Yehova wa makamu. |
|
GENESIS 2:7 |
Ndipo Yehova Mulungu anaumba munthu ndi dothi lapansi, nauzira mpweya wa moyo m'mphuno mwace; munthuyo nakhala wamoyo. |
|
YOHANE 3:3-5 |
[3] Yesu anayankha nati kwa iye, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwatsopano, sakhoza kuona Ufumu wa Mulungu.[4] Nikodemoananena kwa iye, Munthu akhoza bwanji kubadwa atakalamba? Kodi akhoza kulowanso m'mimba ya amace ndi kubadwa?[5] Yesu anayankha, Indetu, indetu, ndinena ndi iwe, Ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu, sakhoza kulowa ufumu wa Mulungu. |
|
AHEBRI 12:14 |
Londolani mtendere ndi anthu onse, ndi ciyeretso cimene, akapanda ici, palibe mmodzi adzaona Ambuye: |
|
CHIVUMBULUTSO 17:18 |
Ndipo mkaziyo unamuona, ndiye mudzi waukuru, wakucita ufumu pa mafumu a dziko. |
|
MATEYU 16:18 |
Ndiponso Ine ndinena kwa iwe, kuti iwe ndiwe Petro, ndipo pa thanthwe ili ndidzakhazika Mpingo wanga; ndipo makomo a dziko la akufa sadzaulaka uwo. |
|
GENESIS 1:1 |
PACIYAMBI Mulungu adalenga kumwamba ndi dziko lapansi. |
|
EKSODO 15:3 |
Yehova ndiye wankhondo; Dzina lace ndiye Yehova. |
|
CHIVUMBULUTSO 17:9 |
Pano pali mtima wakukhaia nayo nzeru. Mitu isanu ndi iwiri ndiyo mapiri asanu ndi awiri amene mkazi akhalapo; |
|
AFILIPI 4:6-7 |
[6] Musadere nkhawa konse; komatu m'zonse ndi pemphero, ndi pembedzero, pamodzi ndi ciyamiko, zopempha zanu zidziwike kwa Mulungu.[7] Ndipo mtendere wa Mulungu wakupambana cidziwitso conse, udzasunga mitima yanu ndi maganizo anu mwa Kristu Yesu. |
|
AGALATIYA 4:19 |
Tiana tanga, amene ndirikumvanso zowawa za kubala inu, kufikira Kristu aumbika mwa inu, |
|
1 PETRO 3:15 |
koma mumpatulikitse Ambuye Kristu m'mitima yanu; okonzeka nthawi zonse kucita codzikanira pa yense wakukufunsani cifukwa ca ciyembekezo ciri mwa inu, komatu ndi cifatsondi mantha; |
|
CHIVUMBULUTSO 17:1 |
Ndipo anadza mmodzi mwa angelo asanu ndi awiri akukhala nazo mbale zisanu ndi ziwiri, nalankhula ndi ine, nanena, Idza kuno, ndidzakuonetsa citsutso ca mkazi wacigololo wamkuru, wakukhala pa madzi ambiri, |
|
MATEYU 18:15-18 |
[15] Ndipo ngati mbale wako akucimwira iwe, pita, numlangize pa nokha iwe ndi iye; ngati akumvera iwe, wambweza mbale wako.[16] Koma ngati samvera, onjeza kutenga ndi iwe wina mmodzi kapena awiri, kuti atsimikizidwe mau onse pakamwa pa mboni ziwiri kapena zitatu.[17] Ndipo ngati iye samvera iwo, uuze Mpingo; ndipo ngati iye samveranso Mpingowo, akhale kwa iwe monga wakunja ndi wamsonkho.[18] Indetu ndinena kwa inu, Ziri zonse mukazimanga pa dziko lapansi zidzakhala zomangidwa Kumwamba: ndipo ziri zonse mukazimasula pa dziko lapansi, zidzakhala zomasulidwa Kumwamba. |
|
AEFESO 1:22-23 |
[22] ndipo 3 anakonza zonse pansi pa mapazi ace, nampatsa iye 4 akhale mutu pamtu pa zonse,[23] 5 kwa Eklesia amene ali thupi lace, 6 mdzazidwe wa iye amene adzazazonse m'zonse. |
|
AEFESO 5:23 |
Pakuti mwamuna ndiye mutu wa mkazi, monganso Kristu ndiye mutu wa Eklesia, ali yekha Mpulumutsi wa thupilo. |
|
MACHITIDWE A ATUMWI 4:32 |
Ndipo unyinji wa iwo akukhulupira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananena mmodzi kuti kanthu ka cuma anali naco ndi kace ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana. |
|
1 AKORINTO 1:10 |
Koma ndikudandaulirani inu, abale, mwa dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu, kuti munene cimodzimodzi inu nonse, ndi kuti pasakhale malekano pakati pa inu; koma mumangike mu mtima womwewo ndi m'ciweruziro comweco. |
|
YOHANE 12:48 |
12 iye amene akaniza Ine, ndi kusalandira mau anga, ali naye womweruza iye; 13 mau amene ndalankhula, iwowa adzamweruza tsiku lomariza. |
|
YOHANE 14:28 |
Mwamva kuti Ine ndinanena kwa inu, 6 Ndimuka, ndipo ndidza kwa inu. Mukadandikonda Ine, mukadakondwera kuti ndipita kwa Atate; 7 pakuti Atate ali wamkuru ndi Ine. |
|
AHEBRI 1:14 |
Kodi siiri yonse mizimu yotumikira, yotumidwa kuti itumikire iwo amene adzalowa cipulumutso? |
|
MATEYU 18:10 |
Yang'anirani kuti musanyoze mmodzi wa ang'ono awa; pakuti ndinena kwa inu, kuti angelo ao apenya cipenyere nkhope ya Atate wanga wa Kumwamba. [ |
|
AEFESO 6:12 |
Cifukwa kuti kulimbana kwathu sitilimbana nao mwazi ndi thupi, komatu nao maukulu, ndi maulamuliro, ndi akucita zolimbika a dziko lapansi a mdima uno, ndi a uzimu a coipa m'zakumwamba. |
|
YOHANE 3:16 |
Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi kotero, kuti anapatsa Mwana wace wobadwa yekha, kuti yense wakukhulupirira iye asatayike, koma akhale nao moyo wosatha. |
|
YOHANE 17:17 |
Patulani iwo m'coonadi; mau anu ndi coonadi. |
|
CHIVUMBULUTSO 2:9 |
Ndidziwa cisautso cako, ndi umphawi wako (komatu uli wacuma), ndi mwano wa iwo akunena za iwo okha kuti ali Ayuda, osakhala Ayuda, komatu sunagoge wa Satana. |
|
MASALIMO 68:5 |
Mulungu, mokhala mwace mayera, Ndiye Atate wa ana amasiye, ndi woweruza wa akazi amasiye. |
|
MASALIMO 146:9 |
Yehova asunga alendo; Agwiriziza mwana wamasiye mkazi wamasiye; Koma akhotetsa njira ya oipa. |
|
AGALATIYA 2:10 |
pokhapo kuti tikumbukile aumphawi; ndico comwe ndinafulumira kucicita. |
|
AROMA 3:23 |
pakuti onse anacimwa, naperewera pa ulemerero wa Mulungu; |
|
Chewa Bible (BL) 1992 |
Zambia Bible Society, Malawi Bible Society and Zimbabwe Bible Society |