|
|
|
|
|
|
|
|
|
|
Sakani
|
|
MATEYU 2:11 |
Pofika ku nyumbayo, anaona mwanayo pamodzi ndi amayi ake Mariya, ndipo anagwada namulambira Iye. Pomwepo anamasula chuma chawo ndi kupereka mphatso zawo za ndalama zagolide, lubani ndi mure.
|
MATEYU 14:33 |
Pamenepo amene anali mʼbwato anamulambira Iye, nati, “Zoonadi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”
|
MATEYU 15:9 |
Amandilambira Ine kwachabe ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.’ ”
|
MATEYU 28:9 |
Mwadzidzidzi Yesu anakumana nawo nati, “Moni.” Iwo anabwera kwa Iye, nagwira mapazi ake namulambira.
|
MATEYU 28:17 |
Atamuona Iye, anamulambira; koma ena anakayika.
|
MARKO 7:7 |
Amandilambira Ine kwachabe; ndi kuphunzitsa malamulo ndi malangizo a anthu.
|
MARKO 15:19 |
Ndipo anamugogoda pa mutu mobwerezabwereza ndi ndodo ndi kumulavulira. Anamugwadira ndi kumulambira Iye.
|
LUKA 4:7 |
Ngati mutandilambira, zonsezi zidzakhala zanu.”
|
LUKA 24:52 |
Pamenepo anamulambira Iye ndipo anabwerera ku Yerusalemu ndi chimwemwe chachikulu.
|
YOHANE 9:38 |
Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.
|
MACHITIDWE A ATUMWI 10:25 |
Petro akulowa mʼnyumba, Korneliyo anakumana naye ndipo anadzigwetsa pa mapazi ake namulambira.
|
Chewa Bible 2016 |
Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® |
|