MATEYU 3:17 |
ndipo onani, mau akuchokera kumiyamba akuti, Uyu ndiye mwana wanga wokondedwa, mwa Iyeyu ndikondwera.
|
MATEYU 12:18 |
Taona mnyamata wanga, amene ndinamsankha, wokondedwa wanga, amene moyo wanga ukondwera naye; pa Iye ndidzaika Mzimu wanga, ndipo Iye adzalalikira chiweruzo kwa akunja.
|
MATEYU 17:5 |
Akali chilankhulire, onani, mtambo wowala unawaphimba iwo: ndipo onani, mau ali kunena mumtambo, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa, mwa iyeyu ndikondwera, mverani Iye.
|
MARKO 1:11 |
ndipo mau anatuluka m'thambo, Mwana wanga wokondedwa ndiwe, mwa Iwe ndikondwera bwino.
|
MARKO 9:7 |
Ndipo panadza mtambo wakuwaphimba iwo; ndipo mau munatuluka m'mtambomo, kuti, Uyu ndiye Mwana wanga wokondedwa; mverani Iye.
|
MARKO 12:6 |
Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wake wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamchitira ulemu mwana wanga.
|
LUKA 3:22 |
ndipo Mzimu Woyera anatsika ndi maonekedwe a thupi lake ngati nkhunda, nadza pa Iye; ndipo munatuluka mau m'thambo, kuti, Iwe ndiwe Mwana wanga wokondedwa, mwa Iwe ndikondwera.
|
LUKA 7:2 |
Ndipo kapolo wa kenturiyo, wokondedwa naye, anadwala, nafuna kutsirizika.
|
AROMA 9:25 |
Monga atinso mwa Hoseya, Amene sanakhala anthu anga, ndidzawatcha anthu anga; ndi iye amene sanali wokondedwa, wokondedwa.
|
AROMA 16:5 |
ndipo mupereke moni kwa Mpingo wa Ambuye wa m'nyumba mwao. Moni kwa Epeneto wokondedwa wanga, ndiye chipatso choundukula cha Asiya cha kwa Khristu.
|
AROMA 16:8 |
Moni kwa Ampiliato wokondedwa wanga mwa Ambuye.
|
AROMA 16:9 |
Moni kwa Urbano wantchito mnzathu mwa Khristu, ndi Stakisi wokondedwa wanga.
|
AROMA 16:12 |
Moni kwa Trifena, ndi Trifosa amene agwiritsa ntchito mwa Ambuye. Moni kwa Perisi, wokondedwayo amene anagwiritsa ntchito zambiri mwa Ambuye.
|
1 AKORINTO 4:17 |
Chifukwa cha ichi ndatuma kwa inu Timoteo, ndiye mwana wanga wokondedwa ndi wokhulupirika mwa Ambuye, amene adzakumbutsa inu njira zanga za mwa Khristu, monga ndiphunzitsa ponsepo m'Mipingo yonse.
|
AEFESO 1:6 |
kuti uyamikidwe ulemerero wa chisomo chake, chimene anatichitira ife kwaufulu mwa Wokondedwayo.
|
AEFESO 6:21 |
Koma kuti mukadziwe inunso za kwa ine, zimene ndichita, zinthu zonse adzakuzindikiritsani Tikiko mbale wokondedwayo, ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye;
|
AKOLOSE 1:7 |
monga momwe munaphunzira kwa Epafra kapolo mnzathu wokondedwa, ndiye mtumiki wokhulupirika wa Khristu chifukwa cha ife;
|
AKOLOSE 4:7 |
Zonse za kwa ine adzakuzindikiritsani Tikiko, mbale wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika ndi kapolo mnzanga mwa Ambuye:
|
AKOLOSE 4:9 |
pamodzi ndi Onesimo, mbale wokhulupirika ndi wokondedwa, amene ali wa kwa inu. Zonse za kuno adzakuzindikiritsani inu.
|
AKOLOSE 4:14 |
Akupatsani moni Luka sing'anga wokondedwa, ndi Dema.
|
2 TIMOTEO 1:2 |
kwa Timoteo, mwana wanga wokondedwa: Chisomo, chifundo, mtendere za kwa Mulungu Atate ndi Khristu Yesu Ambuye wathu.
|
FILEMONI 1:1 |
Paulo, wandende wa Khristu Yesu, ndi Timoteo mbaleyo, kwa Filemoni wokondedwayo ndi wantchito mnzathu,
|
FILEMONI 1:16 |
osatinso monga kapolo, koma woposa kapolo, mbale wokondedwa, makamaka ndi ine, koma koposa nanga ndi iwe, m'thupi, ndiponso mwa Ambuye.
|
2 PETRO 1:17 |
Pakuti analandira kwa Mulungu Atate ulemu ndi ulemerero, pakumdzera Iye mau otere ochokera ku ulemerero waukulu, Uyu ndi Mwana wanga wokondedwa, amene Ine ndikondwera naye;
|
2 PETRO 3:15 |
Ndipo yesani kulekerera kwa Ambuye wathu chipulumutso; monganso mbale wathu wokondedwa Paulo, monga mwa nzeru zopatsidwa kwa iye, anakulemberani;
|
3 YOHANE 1:1 |
Mkuluyo kwa Gayo wokondedwayo, amene ndikondana naye m'choonadi.
|
3 YOHANE 1:2 |
Wokondedwa, ndipemphera kuti pa zonse ulemere, nukhale bwino, monga mzimu wako ulemera.
|
3 YOHANE 1:5 |
Wokondedwa, uchita chokhulupirika nacho chilichonse, uwachitira abale ndi alendo omwe;
|
3 YOHANE 1:11 |
Wokondedwa, usatsanza chili choipa komatu chimene chili chokoma. Iye wakuchita chokoma achokera kwa Mulungu; iye wakuchita choipa sanamuona Mulungu.
|
CHIVUMBULUTSO 20:9 |
Ndipo anakwera nafalikira m'dziko, nazinga tsasa la oyera mtima ndi mudzi wokondedwawo: ndipo unatsika moto wakumwamba nuwanyeketsa.
|
Chewa Bible 2014 |
Bible Society of Malawi |