1 |
Ndipo pamene anamasula chizindikiro chachisanu ndi chiwiri, munali chete m'Mwamba monga mwa nthawi ya ora latheka. |
2 |
Ndipo ndinaona angelo asanu ndi awiri amene amaimirira pamaso pa Mulungu; ndipo anawapatsa malipenga asanu ndi awiri. |
3 |
Ndipo anadza mngelo wina, naima pa guwa la nsembe, nakhala nacho chotengera cha zofukiza chagolide; ndipo anampatsa zofukiza zambiri, kuti aziike pamodzi ndi mapemphero a oyera mtima onse pa guwa la nsembe lagolide, lokhala kumpando wachifumu. |
4 |
Ndipo utsi wa zofukiza, pamodzi ndi mapemphero a oyera mtima unakwera kutuluka m'dzanja la mngelo, pamaso pa Mulungu. |
5 |
Ndipo mngeloyo anatenga mbale ya zofukiza, naidzaza ndi moto wopala pa guwa la nsembe, nauponya pa dziko lapansi; ndipo panakhala mabingu, ndi mau, ndi mphezi, ndi chivomezi. |
6 |
Ndipo angelo asanu ndi awiri akukhala nao malipenga anadzikonzera kuti aombe. |
7 |
Ndipo woyamba anaomba lipenga, ndipo panakhala matalala ndi moto, zosanganiza ndi mwazi, ndipo anazitaya pa dziko lapansi; ndipo limodzi la magawo atatu a dziko lidapserera, ndipo limodzi la magawo atatu a mitengo lidapserera, ndipo msipu wonse udapserera. |
8 |
Ndipo mngelo wachiwiri anaomba lipenga, ndipo monga ngati phiri lalikulu lakupserera ndi moto linaponyedwa m'nyanja; ndipo limodzi la magawo atatu a nyanja linasanduka mwazi; |
9 |
ndipo lidafa limodzi la magawo atatu a zolengedwa zili m'nyanja, zokhala ndi moyo; ndipo limodzi la magawo atatu a zombo lidaonongeka. |
10 |
Ndipo mngelo wachitatu anaomba lipenga, ndipo idagwa kuchokera kumwamba nyenyezi yaikulu, yoyaka ngati muuni, ndipo idagwa pa limodzi la magawo atatu a mitsinje, ndi pa akasupe amadzi; |
11 |
ndipo dzina lake la nyenyeziwo alitcha Chowawa; ndipo limodzi la magawo atatu a madzi lidasanduka chowawa; ndipo anthu ambiri adafa pakumwa madzi, pakuti asananduka owawa. |
12 |
Ndipo mngelo wachinai anaomba lipenga, ndipo limodzi la magawo atatu a dzuwa linagwidwa, ndi limodzi la magawo atatu a mwezi, ndi limodzi la magawo atatu a nyenyezi; kuti limodzi la magawo ao atatu lidetsedwe, ndi kuti limodzi la magawo ake atatu a usana lisawale, ndi usiku momwemo. |
13 |
Ndipo ndinaona, ndipo ndinamva chiombankhanga chilikuuluka pakati pa mwamba, ndi kunena ndi mau akulu, Tsoka, tsoka, tsoka, iwo akukhala padziko, chifukwa cha mau otsala a lipenga la angelo atatu asanaombe.
|
Chewa Bible 2014 |
Bible Society of Malawi |
|
|
|
|
|
|
|
|
|
|
CHIVUMBULUTSO 8:1 |
CHIVUMBULUTSO 8:2 |
CHIVUMBULUTSO 8:3 |
CHIVUMBULUTSO 8:4 |
CHIVUMBULUTSO 8:5 |
CHIVUMBULUTSO 8:6 |
CHIVUMBULUTSO 8:7 |
CHIVUMBULUTSO 8:8 |
CHIVUMBULUTSO 8:9 |
CHIVUMBULUTSO 8:10 |
CHIVUMBULUTSO 8:11 |
CHIVUMBULUTSO 8:12 |
CHIVUMBULUTSO 8:13 |
|
|
|
|
|
|
CHIVUMBULUTSO 1 / CHI 1 |
CHIVUMBULUTSO 2 / CHI 2 |
CHIVUMBULUTSO 3 / CHI 3 |
CHIVUMBULUTSO 4 / CHI 4 |
CHIVUMBULUTSO 5 / CHI 5 |
CHIVUMBULUTSO 6 / CHI 6 |
CHIVUMBULUTSO 7 / CHI 7 |
CHIVUMBULUTSO 8 / CHI 8 |
CHIVUMBULUTSO 9 / CHI 9 |
CHIVUMBULUTSO 10 / CHI 10 |
CHIVUMBULUTSO 11 / CHI 11 |
CHIVUMBULUTSO 12 / CHI 12 |
CHIVUMBULUTSO 13 / CHI 13 |
CHIVUMBULUTSO 14 / CHI 14 |
CHIVUMBULUTSO 15 / CHI 15 |
CHIVUMBULUTSO 16 / CHI 16 |
CHIVUMBULUTSO 17 / CHI 17 |
CHIVUMBULUTSO 18 / CHI 18 |
CHIVUMBULUTSO 19 / CHI 19 |
CHIVUMBULUTSO 20 / CHI 20 |
CHIVUMBULUTSO 21 / CHI 21 |
CHIVUMBULUTSO 22 / CHI 22 |