1 |
Nanga tsono achuma inu, lirani ndi kuchema chifukwa cha masautso anu akudza pa inu. |
2 |
Chuma chanu chaola ndi zovala zanu zajiwa ndi njenjete. |
3 |
Golide wanu ndi siliva wanu zachita dzimbiri, ndipo dzimbiri lake lidzachita mboni zoneneza inu, ndipo zidzadya nyama yanu ngati moto. Mwadzikundikira chuma masiku otsiriza. |
4 |
Taonani, mphotho ya antchitowo anasenga m'minda yanu, yosungidwa ndi inu powanyenga, ifuula; ndipo mafuulo a osengawo adalowa m'makutu a Ambuye wa makamu. |
5 |
Mwadyerera padziko, ndipo mwachita zokukondweretsani; mwadyetsa mitima yanu m'tsiku lakupha. |
6 |
Munamtsutsa, munapha wolungamayo, iye sakaniza inu. |
7 |
Potero, lezani mtima, abale, kufikira kudza kwake kwa Ambuye. Taonani, wolima munda alindira chipatso chofunikatu cha dziko, ndi kuleza mtima nacho kufikira chikalandira mvula ya chizimalupsa ndi masika. |
8 |
Lezani mtima inunso, limbitsani mitima yanu; pakuti kudza kwake kwa Ambuye kuyandikira. |
9 |
Musaipidwe wina ndi mnzake, abale, kuti mungaweruzidwe. Taonani, woweruza aima pakhomo. |
10 |
Tengani, abale, chitsanzo cha kumva zowawa ndi kuleza mtima, aneneri amene analankhula m'dzina la Ambuye. |
11 |
Taonani tiwayesera odala opirirawo; mudamva za chipiriro cha Yobu, ndipo mwaona chitsiriziro cha Ambuye, kuti Ambuye ali wodzala chikondi, ndi wachifundo. |
12 |
Koma makamaka, abale anga, musalumbire, kungakhale kutchula kumwamba kapena dziko, kapena lumbiro lina lililonse; koma inde wanu akhale inde, ndi iai wanu akhale iai; kuti mungagwe m'chiweruziro. |
13 |
Kodi wina wa inu akumva zowawa? Apemphere. Kodi wina asekera? Aimbire. |
14 |
Pali wina kodi adwala mwa inu? Adziitanire akulu a Mpingo, ndipo apemphere pa iye, atamdzoza ndi mafuta m'dzina la Ambuye: |
15 |
ndipo pemphero la chikhulupiriro lidzapulumutsa wodwalayo, ndipo Ambuye adzamuukitsa; ndipo ngati adachita machimo adzakhululukidwa kwa iye. |
16 |
Chifukwa chake muvomerezane wina ndi mnzake machimo anu, ndipo mupempherere wina kwa mnzake kuti muchiritsidwe. Pemphero la munthu wolungama likhoza kwakukulu m'machitidwe ake. |
17 |
Eliya anali munthu wakumva zomwezi tizimva ife, ndipo anapemphera chipempherere kuti isavumbe mvula; ndipo siinagwa mvula pa dziko zaka zitatu kudza miyezi isanu ndi umodzi. |
18 |
Ndipo anapempheranso; ndipo m'mwamba munatsika mvula, ndi dziko lidabala zipatso zake. |
19 |
Abale anga, ngati wina wa inu asochera posiyana ndi choonadi, ndipo ambweza iye mnzake; |
20 |
azindikire, kuti iye amene abweza wochimwa kunjira yake yosochera adzapulumutsa munthu kwa imfa, ndipo adzavundikira machimo aunyinji.
|
Chewa Bible 2014 |
Bible Society of Malawi |
|
|
|
|
|
|
|
|
|
|
YAKOBO 5:1 |
YAKOBO 5:2 |
YAKOBO 5:3 |
YAKOBO 5:4 |
YAKOBO 5:5 |
YAKOBO 5:6 |
YAKOBO 5:7 |
YAKOBO 5:8 |
YAKOBO 5:9 |
YAKOBO 5:10 |
YAKOBO 5:11 |
YAKOBO 5:12 |
YAKOBO 5:13 |
YAKOBO 5:14 |
YAKOBO 5:15 |
YAKOBO 5:16 |
YAKOBO 5:17 |
YAKOBO 5:18 |
YAKOBO 5:19 |
YAKOBO 5:20 |
|
|
|
|
|
|
YAKOBO 1 / YAK 1 |
YAKOBO 2 / YAK 2 |
YAKOBO 3 / YAK 3 |
YAKOBO 4 / YAK 4 |
YAKOBO 5 / YAK 5 |